Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 9:15 - Buku Lopatulika

Amitundu anagwa m'mbuna imene anaikumba, lakodwa phazi lao muukonde anautchera.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Amitundu anagwa m'mbuna imene anaikumba, lakodwa phazi lao muukonde anautcha.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Akunja agwera m'mbuna yokumba iwo omwe. Phazi lao lakodwa mu ukonde wobisika wotcha iwo omwe.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mitundu ya anthu yagwa mʼdzenje limene yakumba; mapazi awo akodwa mu ukonde umene anawubisa.

Onani mutuwo



Masalimo 9:15
11 Mawu Ofanana  

Ndipo apereke nsembe zachiyamiko, nafotokozere ntchito zake ndi kufuula mokondwera.


Ndidzaimbira Yehova, pakuti anandichitira zokoma.


Tsopano ndidziwa kuti Yehova apulumutsa wodzozedwa wake; adzamvomereza mu Mwamba mwake moyera ndi mphamvu ya chipulumutso cha dzanja lake lamanja.


Chimgwere modzidzimutsa chionongeko; ndipo ukonde wake umene anautcha umkole yekha mwini, agwemo, naonongeke m'mwemo.


Ndipo moyo wanga udzakondwera mwa Yehova; udzasekera mwa chipulumutso chake.


Lupanga lao lidzalowa m'mtima mwao momwe, ndipo mauta ao adzathyoledwa.


Ananditchera ukonde apo ndiyenda; moyo wanga wawerama. Anandikumbira mbuna patsogolo panga; anagwa m'kati mwake iwo okha.


Ndipo anawabwezera zopanda pake zao, nadzawaononga m'choipa chao; Yehova Mulungu wathu adzawaononga.


Wofesa zosalungama adzakolola tsoka; ndipo nthyole ya mkwiyo wake idzalephera.


Zoipa zakezake zidzagwira woipa; adzamangidwa ndi zingwe za uchimo wake.