Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 86:1 - Buku Lopatulika

Tcherani khutu lanu Yehova, mundiyankhe; pakuti ine ndine wozunzika ndi waumphawi.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Tcherani khutu lanu Yehova, mundiyankhe; pakuti ine ndine wozunzika ndi waumphawi.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Tcherani khutu, Inu Chauta, ndipo mundiyankhe, pakuti ndine wosauka ndi wosoŵa.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndimvereni Yehova ndipo mundiyankhe, pakuti ndine wosauka ndi wosowa.

Onani mutuwo



Masalimo 86:1
19 Mawu Ofanana  

Mwapenya; pakuti mumayang'anira chivutitso ndi chisoni kuti achipereke m'manja mwanu; waumphawi adzipereka kwa Inu; wamasiye mumakhala mthandizi wake.


Yehova, imvani pemphero langa, ndipo mfuu wanga ufikire Inu.


anasamalira pemphero la iwo akusowa konse, osapepula pemphero lao.


Mundichotsere chotonza, ndi chimpepulo; pakuti ndinasunga mboni zanu.


Ndidziwa kuti Yehova adzanenera wozunzika mlandu, ndi kuweruzira aumphawi.


Ndifuula nalo liu langa kwa Yehova; ndi mau anga ndipemba kwa Yehova.


Ine ndinakuitanani, pakuti mudzandiyankha, Mulungu; tcherani khutu lanu kwa ine, imvani mau anga.


Cheukirani ine ndipo ndichitireni chifundo; pakuti ndili wounguluma ndi wozunzika.


Munditcherere khutu lanu; ndipulumutseni msanga. Mundikhalire ine thanthwe lolimba, nyumba yamalinga yakundisunga.


Munthu uyu wozunzika anafuula, ndipo Yehova anamumva, nampulumutsa m'masautso ake onse.


Ndipo ine ndine wozunzika ndi waumphawi; koma Ambuye andikumbukira ine. Inu ndinu mthandizi wanga, ndi Mpulumutsi wanga, musamachedwa, Mulungu wanga.


Tcherani makutu anu, Yehova, nimumve; tsegulani maso anu, Yehova, nimuone; ndi kumva mau onse a Senakeribu, amene watumiza kumtonza Mulungu wamoyo.


Pakuti zonsezi mkono wanga wazilenga, momwemo zonsezi zinaoneka, ati Yehova; koma ndidzayang'anira munthu uyu amene ali waumphawi, ndi wa mzimu wosweka, nanthunthumira ndi mau anga.


Mulungu wanga, tcherani khutu, nimumvere, tsegulani maso anu, nimupenye zopasuka zathu, ndi mzinda udatchedwawo dzina lanu; pakuti dzina lanu; pakuti sititula mapembedzero athu pamaso panu, chifukwa cha ntchito zathu zolungama, koma chifukwa cha zifundo zanu zochuluka.


Odala ali osauka mumzimu; chifukwa uli wao Ufumu wa Kumwamba.


Mzimu wa Ambuye uli pa Ine, chifukwa chake Iye anandidzoza Ine ndiuze anthu osauka Uthenga Wabwino: anandituma Ine kulalikira am'nsinga mamasulidwe, ndi akhungu kuti apenyanso, kutulutsa ndi ufulu ophwanyika,


Mverani, abale anga okondedwa; kodi Mulungu sanasankhe osauka a dziko lapansi akhale olemera ndi chikhulupiriro, ndi olowa nyumba a ufumu umene adaulonjeza kwa iwo akumkonda Iye?