Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 85:7 - Buku Lopatulika

Tionetseni chifundo chanu, Yehova, tipatseni chipulumutso chanu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Tionetseni chifundo chanu, Yehova, tipatseni chipulumutso chanu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Tiwonetseni chikondi chanu chosasinthika, Inu Chauta, ndipo mutipulumutse.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Tionetseni chikondi chanu chosatha, Inu Yehova, ndipo tipatseni chipulumutso chanu.

Onani mutuwo



Masalimo 85:7
5 Mawu Ofanana  

Wopereka nsembe yachiyamiko andilemekeza Ine; ndipo kwa iye wosunga mayendedwe ake ndidzamuonetsa chipulumutso cha Mulungu.


Ndidzamkhutitsa ndi masiku ambiri, ndi kumuonetsera chipulumutso changa.


Atero Yehova: M'malo muno, m'mene muti, Ndi bwinja, mopanda munthu, mopanda nyama, m'mizinda ya Yuda, m'makwalala a Yerusalemu, amene ali bwinja, opanda munthu, opanda wokhalamo, opanda nyama,


mudzamvekanso mau akukondwa ndi mau akusekera, mau a mkwati ndi mau a mkwatibwi, mau a iwo akuti, Myamikireni Yehova wa makamu, pakuti Yehova ndiye wabwino, chifundo chake nchosatha; ndi a iwo akutengera nsembe zoyamikira m'nyumba ya Yehova. Pakuti ndidzabweza undende wa dziko monga poyamba, ati Yehova.


Ndipo ndidzakuchitirani inu chifundo, kuti iye akuchitireni inu chifundo, nakubwezereni inu kudziko lanu.