Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 84:1 - Buku Lopatulika

Pokhala Inu mpotikonda ndithu, Yehova wa makamu!

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Pokhala Inu mpotikonda ndithu, Yehova wa makamu!

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Malo amene mumakhalamo, Inu Chauta Wamphamvuzonse, ndi okoma kwambiri.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Malo anu okhalamo ndi okomadi, Inu Yehova Wamphamvuzonse!

Onani mutuwo



Masalimo 84:1
17 Mawu Ofanana  

Ndipo anati, Chifukwa chake tamverani mau a Yehova, Ndinaona Yehova alikukhala pa mpando wake wachifumu, ndi khamu lonse lakumwamba lili chilili m'mbali mwake, ku dzanja lamanja ndi lamanzere.


Inu ndinu Yehova, nokhanu; mwalenga thambo, kumwambamwamba, ndi khamu lao lonse, dziko lapansi, ndi zonse zili pomwepo, nyanja ndi zonse zili m'mwemo, ndi Inu muzisunga zamoyo zonsezi, ndi khamu lakumwamba lilambira Inu.


Ndinakondwera m'mene ananena nane, Tiyeni kunyumba ya Yehova.


kufikira nditapezera Yehova malo, chokhalamo Wamphamvuyo wa Yakobo?


Chinthu chimodzi ndinachipempha kwa Yehova, ndidzachilondola ichi, Kuti ndikhalitse m'nyumba ya Yehova masiku onse a moyo wanga, kupenya kukongola kwake kwa Yehova ndi kufunsitsa mu Kachisi wake.


Adzakhuta kwambiri ndi zonona za m'nyumba mwanu, ndipo mudzawamwetsa mu mtsinje wa zokondweretsa zanu.


Monga nswala ipuma wefuwefu kukhumba mitsinje; motero moyo wanga upuma wefuwefu kukhumba Inu, Mulungu.


Tumizirani kuunika kwanu ndi choonadi chanu zinditsogolere; zindifikitse kuphiri lanu loyera, kumene mukhala Inuko.


Yehova, Ambuye wathu, dzina lanu liposadi nanga padziko lonse lapansi! Inu amene munaika ulemerero wanu pa thambo la kumwamba.


Imbitsirani Mulungu ndiye mphamvu yathu; fuulirani kwa Mulungu wa Yakobo.