Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 79:8 - Buku Lopatulika

Musakumbukire motitsutsa mphulupulu za makolo athu; nsoni zokoma zanu zitipeze msanga, pakuti tafooka kwambiri.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Musakumbukire motitsutsa mphulupulu za makolo athu; nsoni zokoma zanu zitipeze msanga, pakuti tafooka kwambiri.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Musatilange ife chifukwa cha machimo a makolo athu. Mutichitire chifundo msanga, chifukwa tatsitsidwa kwambiri.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Musatilange chifukwa cha machimo a makolo athu chifundo chanu chibwere msanga kukumana nafe, pakuti tili ndi chosowa chachikulu.

Onani mutuwo



Masalimo 79:8
18 Mawu Ofanana  

Koma iwo adzabweranso kuno mbadwo wachinai: pakuti mphulupulu za Aamori sizinakwaniridwe.


Ndipo mkaziyo ananena ndi Eliya, Ndili nawe chiyani munthu iwe wa Mulungu? Kodi wadza kwa ine kundikumbutsa tchimo langa, ndi kundiphera mwana wanga?


Iye anawalanditsa kawirikawiri; koma anapikisana ndi Iye mwa uphungu wao, ndi mphulupulu zao zinawafoketsa.


Yehova asunga opusa; ndidafooka ine, koma anandipulumutsa.


Mukasunga mphulupulu, Yehova, adzakhala chilili ndani, Ambuye?


Tamverani kufuula kwanga; popeza ndisauka kwambiri; ndilanditseni kwa iwo akundilondola; popeza andipambana.


Pakuti mufika kwa iye ndi madalitso okoma; muika korona wa golide woyengetsa pamutu pake.


Musakumbukire zolakwa za ubwana wanga kapena zopikisana nanu. Mundikumbukire monga mwa chifundo chanu, chifukwa cha ubwino wanu, Yehova.


Ndipo tsopano, muka, tsogolera anthu kunka nao kumene ndinakuuza; taona, mthenga wanga akutsogolera; koma tsiku lakuwazonda Ine ndidzawalanga chifukwa cha kuchimwa kwao.


Musakwiye kopambana, Yehova, musakumbukire zoipa nthawi zonse; taonani, yang'anani ife, tikupembedzani Inu, ife tonse tili anthu anu.


Nati kwa ine, Wobadwa ndi munthu iwe, ndikutumizira kwa ana a Israele, kwa mitundu ya anthu opanduka, amene anapandukana nane; iwo ndi makolo ao anandilakwira mpaka lero lomwe.


Ambuye, monga mwa chilungamo chanu chonse, mkwiyo wanu ndi ukali wanu zitembenuketu, zichoke kumzinda wanu Yerusalemu, phiri lanu lopatulika; pakuti mwa zochimwa zathu, ndi mphulupulu za makolo athu, Yerusalemu ndi anthu anu asanduka chotonza cha onse otizungulira.


Kunena za nsembe za zopereka zanga, aphera nsembe yanyama, naidya; koma Yehova sazilandira; tsopano adzakumbukira mphulupulu yao, nadzalanga zochimwa zao; adzabwerera kunka ku Ejipito.


Anadzivunditsa kwambiri, monga masiku a Gibea; adzakumbukira mphulupulu yao, adzalanga zochimwa zao.


Mlendo wokhala pakati panu adzakulirakulira inu, koma inu mudzacheperachepera.


pakuti machimo ake anaunjikizana kufikira mu Mwamba, ndipo Mulungu anakumbuka zosalungama zake.