Ndipo ndidzaika pa iwo mitundu inai, ati Yehova, lupanga lakupha, agalu akung'amba, mbalame za m'mlengalenga, ndi zilombo zapansi, zakulusa ndi kuononga.
Masalimo 79:2 - Buku Lopatulika Anapereka mitembo ya atumiki anu ikhale chakudya cha mbalame za mlengalenga, nyama ya okondedwa anu anaipereka kwa zilombo za m'dziko. Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 Anapereka mitembo ya atumiki anu ikhale chakudya cha mbalame za mlengalenga, nyama ya okondedwa anu anaipereka kwa zilombo za m'dziko. Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa Ataya mitembo ya atumiki anu kwa mbalame zamumlengalenga, kuti ikhale chakudya chake, ataya matupi a anthu anu oyera mtima kwa zilombo zakuthengo. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Iwo anapereka mitembo ya atumiki anu kwa mbalame zamlengalenga ngati chakudya, matupi a oyera mtima anu kwa zirombo za dziko lapansi. |
Ndipo ndidzaika pa iwo mitundu inai, ati Yehova, lupanga lakupha, agalu akung'amba, mbalame za m'mlengalenga, ndi zilombo zapansi, zakulusa ndi kuononga.
Adzafa ndi imfa zanthenda; sadzaliridwa maliro, sadzaikidwa; adzakhala ngati ndowe panthaka; ndipo adzathedwa lupanga, ndi njala; ndipo mitembo yao idzakhala chakudya cha mbalame za kumlengalenga, ndi zilombo za dziko lapansi.
Ndipo ndidzataya uphungu wa Yuda ndi wa Yerusalemu m'malo ano; ndipo ndidzagwetsa iwo ndi lupanga pamaso pa adani ao, ndi padzanja la iwo amene afuna moyo wao; mitembo yao ndidzapatsa ikhale chakudya cha mbalame za m'mlengalenga, ndi cha zilombo za dziko lapansi.
ndidzapereka iwo m'dzanja la adani ao, ndi m'dzanja la iwo akufuna moyo wao; ndipo mitembo yao idzakhala chakudya cha mbalame za mlengalenga, ndi cha zilombo za padziko lapansi.
Ndipo mitembo ya anthu awa idzakhala zakudya za mbalame za mlengalenga, ndi za zilombo za dziko lapansi; palibe amene adzaziopsa.
Ndipo ndidzatengera anthu zowapsinja, kuti adzayenda ngati anthu akhungu, popeza anachimwira Yehova; ndi mwazi wao udzatsanulidwa ngati fumbi, ndi nyama yao idzanga ndowe.
Ndipo mitembo yanu idzakhala chakudya cha mbalame zonse za m'mlengalenga, ndi zilombo zonse za padziko lapansi, ndipo palibe wakuziingitsa.