Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 79:11 - Buku Lopatulika

Kubuula kwa wandende kufike kuli Inu; monga mwa mphamvu yanu yaikulu lolani ana a imfa atsale.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Kubuula kwa wandende kufike kuli Inu; monga mwa mphamvu yanu yaikulu lolani ana a imfa atsale.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Mumve kubuula kwa anthu am'ndende, muŵasunge ndi mphamvu zanu zazikulu anthu oyenera kuphedwa.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Kubuwula kwa anthu a mʼndende kufike pamaso panu; ndi mphamvu ya dzanja lanu muwasunge amene aweruzidwa kuti aphedwe.

Onani mutuwo



Masalimo 79:11
11 Mawu Ofanana  

kuti amve kubuula kwa wandende; namasule ana a imfa.


Kuti anthu alalikire dzina la Yehova mu Ziyoni, ndi chilemekezo chake mu Yerusalemu;


Chifukwa cha kupasuka kwa ozunzika, chifukwa cha kuusa moyo kwa aumphawi, ndiuka tsopano, ati Yehova; ndidzamlonga mosungika muja alakalakamo.


Pakuti Yehova amvera aumphawi, ndipo sapeputsa am'ndende ake.


Inu Yehova, mutikomere ife mtima; ife talindira Inu; mukhale dzanja lathu m'mawa ndi m'mawa, chipulumutso chathunso m'nthawi ya mavuto.


kuti utsegule maso akhungu, utulutse am'nsinga m'ndende, ndi iwo amene akhala mumdima, atuluke m'nyumba ya kaidi.


Ndipo musatitengere kokatiyesa, koma mutipulumutse kwa woipayo.


Ndipo kwa Iye amene angathe kuchita koposaposatu zonse zimene tizipempha, kapena tiziganiza, monga mwa mphamvu ya kuchita mwa ife,