Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 78:3 - Buku Lopatulika

Zimene tinazimva, ndi kuzidziwa, ndipo makolo athu anatifotokozera.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Zimene tinazimva, ndi kuzidziwa, ndipo makolo athu anatifotokozera.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

zinthu zimene tidazimva ndi kuzidziŵa, zomwe makolo athu adatifotokozera.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

zimene tinazimva ndi kuzidziwa, zimene makolo athu anatiwuza.

Onani mutuwo



Masalimo 78:3
9 Mawu Ofanana  

Taonani, diso langa lachiona chonsechi; m'khutu mwanga ndachimva ndi kuchizindikira.


Mbadwo wina udzalemekezera ntchito zanu mbadwo unzake, ndipo udzalalikira zamphamvu zanu.


Mulungu, tidamva m'makutu mwathu, makolo athu anatisimbira, za ntchitoyo mudaichita masiku ao, masiku akale.


Monga tidamva, momwemo tidapenya m'mzinda wa Yehova wa makamu, m'mzinda wa Mulungu wathu, Mulungu adzaukhazikitsa kunthawi yamuyaya.


ndi kuti ufotokozere m'makutu a ana ako, ndi a zidzukulu zako, chomwe ndidzachita mu Ejipito, ndi zizindikiro zanga zimene ndinaziika pakati pao; kuti mudziwe kuti Ine ndine Yehova.


Ndipo ukauze mwana wako wamwamuna tsikulo, ndi kuti, Nditero chifukwa chomwe Yehova anandichitira ine potuluka ine mu Ejipito.


Wamoyo, wamoyo, iye adzakuyamikani inu, monga ine lero; Atate adzadziwitsa ana ake zoona zanu.