Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 76:1 - Buku Lopatulika

Mulungu adziwika mwa Yuda, dzina lake limveka mwa Israele.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Mulungu adziwika mwa Yuda, dzina lake limveka mwa Israele.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Mulungu ndi wodziŵika m'dziko la Yuda, dzina lake ndi lolemekezeka mu Israele.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mulungu amadziwika mu Yuda; dzina lake ndi lotchuka mu Israeli.

Onani mutuwo



Masalimo 76:1
18 Mawu Ofanana  

Pakufuula ine mundiyankhe, Mulungu wa chilungamo changa; pondichepera mwandikulitsira malo. Ndichitireni chifundo, imvani pemphero langa.


Mulungu wa milungu, Yehova, wanena, aitana dziko lapansi kuyambira kutuluka kwa dzuwa kufikira kulowa kwake.


Ndipulumutseni, Mulungu, mwa dzina lanu, ndipo mundiweruze ndi mphamvu yanu.


Imvani mfuu wanga, Mulungu; mverani pemphero langa.


Atichitire chifundo Mulungu, ndi kutidalitsa, atiwalitsire nkhope yake;


Chifukwa chake ndilamulira kuti anthu ali onse, mtundu uliwonse, ndi a manenedwe ali onse, akunenera molakwira Mulungu wa Sadrake, Mesaki, ndi Abedenego, adzadulidwa nthulinthuli, ndi nyumba zao zidzasanduka dzala; popeza palibe mulungu wina akhoza kulanditsa motero.


Pakuti popita, ndi kuona zinthu zimene muzipembedza, ndipezanso guwa la nsembe lolembedwa potere, KWA MULUNGU WOSADZIWIKA. Chimene muchipembedza osachidziwa, chimenecho ndichilalikira kwa inu.


Koma ngati iwe unenedwa Myuda, nukhazikika palamulo, nudzitamandira pa Mulungu,