Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 73:8 - Buku Lopatulika

Achita zaphwete nalankhula moipa za kusautsa, alankhula modzitama.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Achita zaphwete nalankhula moipa za kusautsa, alankhula modzitama.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Amanyodola ndi kumalankhula zoipa, amadzikuza ndi kumaopseza ena kuti, “Tikupsinjani.”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Iwowo amanyogodola ndi kumayankhula zoyipa; mwa kudzikuza kwawo amaopseza ena nʼkumati, “Tikuponderezani.”

Onani mutuwo



Masalimo 73:8
16 Mawu Ofanana  

Itero mfumu, Asakunyengeni Hezekiya; pakuti sadzakhoza kukulanditsani m'dzanja lake;


Podzikuza woipa apsereza waumphawi; agwe m'chiwembu anapanganacho.


Mafuta ao awatsekereza; m'kamwa mwao alankhula modzikuza.


Ndipo pakamwa panu mwadzikuza pa Ine, ndi kundichulukitsira mau anu ndawamva Ine.


Abwerera, koma si kwa Wam'mwambayo; akunga uta wosakhulupirika; akalonga ao adzagwa ndi lupanga mwa chipongwe cha lilime lao; ichi ndicho adzawasekera m'dziko la Ejipito.


koma makamaka iwo akutsata za thupi, m'chilakolako cha zodetsa, napeputsa chilamuliro; osaopa kanthu, otsata chifuniro cha iwo eni, santhunthumira kuchitira mwano akulu aulemerero;


Pakuti polankhula mau otukumuka opanda pake, anyengerera pa zilakolako za thupi, ndi zonyansa, anthu amene adayamba kupulumuka kwa iwo a mayendedwe olakwa;


Amenewo ndiwo odandaula, oderera, akuyenda monga mwa zilakolako zao (ndipo pakamwa pao alankhula zazikuluzikulu), akutama anthu chifukwa cha kupindula nako.


Ndipo m'dziko lonse la Israele simunapezeke wosula; popeza Afilisti adati, Kuti Aisraele angadzisulire malupanga kapena mikondo;