Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 73:11 - Buku Lopatulika

Namati, Akachidziwa bwanji Mulungu? Kodi Wam'mwambamwamba ali nayo nzeru?

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Namati, Akachidziwa bwanji Mulungu? Kodi Wam'mwambamwamba ali nayo nzeru?

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Amati, “Kodi Mulungu angadziŵe bwanji? Kodi Wopambanazonseyo angadziŵe kanthu kalikonse?”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Iwo amati, “Kodi Mulungu angadziwe bwanji? Kodi Wammwambamwamba angadziwe kalikonse?”

Onani mutuwo



Masalimo 73:11
10 Mawu Ofanana  

Anena m'mtima mwake, Mulungu waiwala; wabisa nkhope yake; sapenya nthawi zonse.


Woipa, monga mwa kudzikuza kwa nkhope yake, akuti, Sadzafunsira. Malingaliro ake onse akuti, Palibe Mulungu.


Mulungu sakadasanthula ichi kodi? Pakuti adziwa zinsinsi za mtima.


Pakamwa pao anena zam'mwamba, ndipo lilime lao liyendayenda m'dziko lapansi.


Ndipo amati, Yehova sachipenya, ndi Mulungu wa Yakobo sachisamalira.


Pamenepo anati kwa ine, Wobadwa ndi munthu iwe, wapenya kodi chochita akulu a nyumba ya Israele mumdima, aliyense m'chipinda chake cha zifanizo? Pakuti ati, Yehova satipenya, Yehova wataya dziko.


Ndipo sanena m'mtima mwao kuti Ine ndikumbukira zoipa zao zonse; tsopano machitidwe ao awazinga; ali pamaso panga.


Ndipo kudzachitika nthawi yomweyi kuti ndidzasanthula Yerusalemu ndi nyali, ndipo ndidzalanga amunawo okhala ndi nsenga, onena m'mtima mwao, Yehova sachita chokoma, kapena kuchita choipa.