Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 72:9 - Buku Lopatulika

Okhala m'chipululu adzagwadira pamaso pake; ndi adani ake adzaluma nthaka.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Okhala m'chipululu adzagwadira pamaso pake; ndi adani ake adzaluma nthaka.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Amaliwongo akuchipululu adzaiŵeramira, adani ake adzadya fumbi.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mafuko a mʼchipululu adzawerama pamaso pake ndipo adani ake adzanyambita fumbi.

Onani mutuwo



Masalimo 72:9
12 Mawu Ofanana  

Ndipo anati Yehova Mulungu kwa njokayo, Chifukwa kuti wachita ichi, wotembereredwa ndiwe wopambana ndi zinyama zonse ndi zamoyo zonse za m'thengo: uziyenda ndi pamimba pako, uzidya fumbi masiku onse a moyo wako:


ndi Baalati, ndi Tamara wa m'chipululu m'dziko muja,


Yehova ananena kwa Ambuye wanga, Khalani padzanja lamanja langa, kufikira nditaika adani anu chopondapo mapazi anu.


Adzaweruza mwa amitundu, adzadzaza dziko ndi mitembo; adzaphwanya mitu m'maiko ambiri.


Udzawathyola ndi ndodo yachitsulo; udzawaphwanya monga mbiya ya woumba.


Onenepa onse a padziko lapansi adzadya nadzagwadira; onse akutsikira kufumbi adzawerama pamaso pake, ndi iye amene sadziwa kusunga moyo wake.


Ndipo mafumu adzakulera, ndi akazi ao aakulu adzakuyamwitsa; iwo adzakugwadira ndi nkhope zao zoyang'ana pansi, nadzaseteka fumbi la m'mapazi ako: ndipo iwe udzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndi iwo amene alindira Ine sadzakhala ndi manyazi.


Adzanyambita fumbi ngati njoka; ngati zokwawa za padziko, adzanjenjemera potuluka m'ngaka mwao; adzafika kwa Yehova Mulungu wao ndi mantha, nadzaopa chifukwa cha iwe.


Koma adani anga aja osafuna kuti ndidzakhala mfumu yao, bwerani nao kuno, nimuwaphe pamaso panga.