Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 69:32 - Buku Lopatulika

Ofatsa anachiona, nakondwera, ndipo inu, ofuna Mulungu, mtima wanu ukhale ndi moyo.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ofatsa anachiona, nakondwera, ndipo inu, ofuna Mulungu, mtima wanu ukhale ndi moyo.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ozunzika aone zimenezo ndipo asangalale, inu amene mumafunafuna Mulungu, mulimbenso mtima.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Wosauka adzaona ndipo adzasangalala, Inu amene mumafunafuna Mulungu, mitima yanu ikhale ndi moyo!

Onani mutuwo



Masalimo 69:32
10 Mawu Ofanana  

Ozunzika adzadya nadzakhuta, adzayamika Yehova iwo amene amfuna, ukhale moyo mtima wako nthawi zonse.


Onenepa onse a padziko lapansi adzadya nadzagwadira; onse akutsikira kufumbi adzawerama pamaso pake, ndi iye amene sadziwa kusunga moyo wake.


Adzawatsogolera ofatsa m'chiweruzo; ndipo adzaphunzitsa ofatsa njira yake.


Moyo wanga udzatamanda Yehova; ofatsa adzakumva nadzakondwera.


Kodi ndidzadya nyama ya ng'ombe, kapena kumwa mwazi wa mbuzi?


Pereka kwa Mulungu nsembe yachiyamiko; numchitire Wam'mwambamwamba chowinda chako.


Ndipo inu tsono muli nacho chisoni tsopano lino, koma ndidzakuonaninso, ndipo mtima wanu udzakondwera, ndipo palibe wina adzachotsa kwa inu chimwemwe chanu.


Ndipo pamene adanena ichi, anaonetsa iwo manja ake ndi nthiti zake. Pamenepo ophunzira anakondwera pakuona Ambuye.