Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 69:23 - Buku Lopatulika

M'maso mwao mude, kuti asapenye; ndipo munjenjemeretse m'chuuno mwao kosalekeza.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

M'maso mwao mude, kuti asapenye; ndipo munjenjemeretse m'chuuno mwao kosalekeza.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Maso ao achite chidima kuti asathe kupenya, ziwuno zao zizinjenjemera kosalekeza.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Maso awo adetsedwe kotero kuti asaonenso ndipo misana yawo ipindike mpaka kalekale.

Onani mutuwo



Masalimo 69:23
12 Mawu Ofanana  

Funsani tsopano, ndi kuona ngati mwamuna aona mwana; chifukwa chanji ndiona mwamuna ndi manja ake pa chuuno chake, monga mkazi alinkubala, ndi nkhope zao zotumbuluka?


Pamenepo padasandulika pa nkhope pake pa mfumu, ndi maganizo ake anamsautsa, ndi mfundo za m'chuuno mwake zinaguluka, ndi maondo ake anaombana.


maso ao adetsedwe, kuti asapenye, ndipo muweramitse msana wao masiku onse.


Pakuti sindifuna, abale, kuti mukhale osadziwa chinsinsi ichi, kuti mungadziyese anzeru mwa inu nokha, kuti kuuma mtima kunadza pang'ono pa Israele, kufikira kudzaza kwa anthu amitundu kunalowa;


koma mitima yao inaumitsidwa; pakuti kufikira lero lomwe lino, pa kuwerenga kwa pangano lakale chophimba chomwechi chikhalabe chosavundukuka, chimene chilikuchotsedwa mwa Khristu.