Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 69:19 - Buku Lopatulika

Mudziwa chotonza changa, ndi manyazi anga, ndi chimpepulo changa. Akundisautsa ali pamaso panu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Mudziwa chotonza changa, ndi manyazi anga, ndi chimpepulo changa. Akundisautsa ali pamaso panu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Inu mumadziŵa m'mene anthu amandinyozera, m'mene amandichititsira manyazi ndi kundichotsera ulemu. Adani anga onse mumaŵadziŵa.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Inu mukudziwa momwe ndanyozedwera, kunyozedwa ndi kuchititsidwa manyazi; adani anga onse ali pamaso panu.

Onani mutuwo



Masalimo 69:19
9 Mawu Ofanana  

Ambuye, chikhumbo changa chonse chili pamaso panu; ndipo kubuula kwanga sikubisika kwa Inu.


Pakuti m'kamwa mwao mulibe mau okhazikika; m'kati mwao m'mosakaza; m'mero mwao ndi manda apululu; lilime lao asyasyalika nalo.


Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu; munthu wazisoni, ndi wodziwa zowawa; ndipo ananyozedwa monga munthu wombisira anthu nkhope zao; ndipo ife sitinamlemekeze.


Yesu anayankha, Ndilibe chiwanda Ine; koma ndilemekeza Atate wanga, ndipo inu mundipeputsa.


Yesu, ameneyo, chifukwa cha chimwemwe choikidwacho pamaso pake, anapirira mtanda, nanyoza manyazi, nakhala padzanja lamanja la mpando wachifumu wa Mulungu.


amene pochitidwa chipongwe sanabwezere chipongwe, pakumva zowawa, sanaopse, koma anapereka mlandu kwa Iye woweruza kolungama;