Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 69:11 - Buku Lopatulika

Ndipo chovala changa ndinayesa chiguduli, koma amandiphera mwambi.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo chovala changa ndinayesa chiguduli, koma amandiphera mwambi.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pamene ndidavala chiguduli kuwonetsa chisoni, ndidasanduka chinthu choŵaseketsa.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

pomwe ndavala chiguduli, anthu amandiseweretsa.

Onani mutuwo



Masalimo 69:11
11 Mawu Ofanana  

pamenepo Ine ndidzalikha Aisraele kuwachotsera m'dziko ndidawapatsali; ndipo nyumba ino ndapatulira dzina langayi ndidzaitaya kosapenyeka; ndipo Israele adzakhala ngati mwambi ndi nkhani pakati pa anthu onse.


Anandiyesanso chitonzo cha anthu; ndipo ndakhala ngati munthu womthira malovu pankhope pake.


Mabondo anga agwedezeka chifukwa cha kusala; ndi mnofu wanga waonda posowa mafuta.


Nthawi imeneyo Yehova ananena ndi Yesaya, mwana wa Amozi, nati, Muka numasule chiguduli m'chuuno mwako, nuchichotse, nuvule nsapato yako kuphazi lako. Ndipo iye anatero, nayenda maliseche, ndi wopanda nsapato.


Ndipo tsiku limenelo Ambuye, Yehova wa makamu, anaitana kulira, ndi kugwa misozi, ndi kumeta, ndi kuvala chiguduli m'chuuno;


Ndipo ndidzawapatsa akhale choopsetsa choipa ku maufumu a dziko lapansi; akhale chitonzo ndi nkhani ndi choseketsa, ndi chitemberero, monse m'mene ndidzawapirikitsiramo.


Mudzimangire chiguduli m'chuuno mwanu, nimulire, ansembe inu; bumani otumikira kuguwa la nsembe inu; lowani, gonani usiku wonse m'chiguduli, inu otumikira Mulungu wanga; pakuti nsembe yaufa ndi nsembe yothira zaletsedwera nyumba ya Mulungu wanu.


Lirani ngati namwali wodzimangira m'chuuno chiguduli, chifukwa cha mwamuna wa unamwali wake.


Ndipo mudzakhala chodabwitsa, ndi nkhani, ndi mwambi, mwa mitundu yonse ya anthu amene Yehova akutsogoleraniko.