Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 66:8 - Buku Lopatulika

Lemekezani Mulungu wathu, mitundu ya anthu inu, ndipo mumveketse liu la chilemekezo chake.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Lemekezani Mulungu wathu, mitundu ya anthu inu, ndipo mumveketse liu la chilemekezo chake.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Lemekezani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthunu, mau omtamanda Iye amveke.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Tamandani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthu, mulole kuti mawu a matamando ake amveke;

Onani mutuwo



Masalimo 66:8
9 Mawu Ofanana  

Ombani m'manja, mitundu yonse ya anthu; fuulirani kwa Mulungu ndi liu la kuimbitsa.


Imbirani ulemerero wa dzina lake; pomlemekeza mumchitire ulemerero.


Fuulirani kwa Yehova, inu, dziko lonse lapansi; kuwitsani ndi kufuulira mokondwera; inde, imbirani zomlemekeza.


mudzamvekanso mau akukondwa ndi mau akusekera, mau a mkwati ndi mau a mkwatibwi, mau a iwo akuti, Myamikireni Yehova wa makamu, pakuti Yehova ndiye wabwino, chifundo chake nchosatha; ndi a iwo akutengera nsembe zoyamikira m'nyumba ya Yehova. Pakuti ndidzabweza undende wa dziko monga poyamba, ati Yehova.


Kondwerani, amitundu inu, ndi anthu ake; adzalipsira mwazi wa atumiki ake, adzabwezera chilango akumuukira, nadzafafanizira zoipa dziko lake, ndi anthu ake.


Zitatha izi ndinamva ngati mau aakulu a khamu lalikulu mu Mwamba, lili kunena, Aleluya; chipulumutso, ndi ulemerero, ndi mphamvu, nza Mulungu wathu;