Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 60:4 - Buku Lopatulika

Koma mwapatsa mbendera akuopa Inu, aikweze chifukwa cha choonadi.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Koma mwapatsa mbendera akuopa Inu, aikweze chifukwa cha choonadi.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Komabe Inu mwatikwezera mbendera ife amene timakuwopani, kuti tisonkhanireko pothaŵa uta wankhondo.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera kuti tisonkhanireko pothawa uta.

Onani mutuwo



Masalimo 60:4
12 Mawu Ofanana  

Tidzafuula mokondwera mwa chipulumutso chanu, ndipo m'dzina la Mulungu wathu tidzakweza mbendera; Yehova akwaniritse mapempho ako onse.


Ndipo pindulani, mu ukulu wanu yendani, kaamba ka choonadi ndi chifatso ndi chilungamo; ndipo dzanja lanu lidzakuphunzitsani zoopsa.


Ndipo Mose anamanga guwa la nsembe, nalitcha dzina lake Yehova Nisi:


Anandifikitsa kunyumba ya vinyo, mbendera yake yondizolimira inali chikondi.


Ndipo Iye adzaimika mbendera ya amitundu, ndipo adzasonkhanitsa oingitsidwa a Israele, namema obalalika a Yuda, kuchokera kumadera anai a dziko lapansi.


Kwezani mbendera paphiri loti see, kwezani mau kwa iwo, kodolani kuti alowe m'zipata za akulu.


Atero Ambuye Yehova, Taona ndidzakodola anthu a mitundu, ndi kukwezera anthu mbendera yanga; ndipo adzabwera nao ana ako aamuna pa chifuwa chao, ndi ana ako aakazi adzatengedwa pa mapewa ao.


Ndipo Iye adzakwezera a mitundu yakutali mbendera, nadzawaimbira mluzu, achokere ku malekezero a dziko; ndipo taonani, iwo adzadza ndi liwiro msangamsanga;


Chomwecho iwo adzaopa dzina la Yehova kuchokera kumadzulo, ndi ulemerero wake kumene kutulukira dzuwa; pakuti pamene mdani adzafika ngati chigumula, mzimu wa Yehova udzamkwezera mbendera yomletsa.