Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 58:2 - Buku Lopatulika

Inde, mumtima muchita zosalungama; padziko lapansi mugawira anthu chiwawa cha m'manja mwanu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Inde, mumtima muchita zosalungama; pa dziko lapansi mugawira anthu chiwawa cha m'manja mwanu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Iyai, mitima yanu imangolingalira zoipa, kuweruza kwanu kosalungama kumadzetsa chiwawa.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ayi, mʼmitima mwanu mumakonzekera zosalungama, ndipo manja anu amatulutsa zachiwawa pa dziko lapansi.

Onani mutuwo



Masalimo 58:2
14 Mawu Ofanana  

Pakuti anakupangirani choipa, anapangana chiwembu, osakhoza kuchichita.


Mulungu aima mu msonkhano wa Mulungu, aweruza pakati pa milungu.


Kodi uyenera kuyanjana ndi Inu mpando wachifumu wa kusakaza, wakupanga chovuta chikhale lamulo?


Ndiponso ndinaona kunja kuno malo akuweruza, komweko kuli zoipa; ndi malo a chilungamo, komweko kuli zoipa.


Tsoka kwa iwo amene alamulira malamulo osalungama, ndi kwa alembi olemba mphulupulu;


Njira ya wolungama ili njira yoongoka; Inu amene muli woongoka, mukonza njira ya wolungama.


Analandira mphotho mwa iwe kukhetsa mwazi, walandira phindu loonjezerapo, wanyengerera anansi ako ndi kuwazunza, ndipo wandiiwala Ine, ati Ambuye Yehova.


Akalonga ake m'kati mwake akunga mimbulu yakumwetula nyama, kukhetsa mwazi, kuononga miyoyo, kuti aone phindu lonyenga.


Ndipo tsopano tiwatcha odzikuza odala, inde iwo ochita zoipa amangidwa ngati nyumba; inde, ayesa Mulungu, napulumuka.