Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 55:1 - Buku Lopatulika

Tcherani khutu pemphero langa, Mulungu; ndipo musadzibisa pa kupemba kwanga.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Tcherani khutu pemphero langa, Mulungu; ndipo musadzibisa pa kupemba kwanga.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Inu Mulungu, tcherani khutu kuti mumve pemphero langa, musabisale pamene ndikukupembani.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mvetserani pemphero langa, Inu Mulungu, musakufulatire kupempha kwanga,

Onani mutuwo



Masalimo 55:1
16 Mawu Ofanana  

Fulumirani ndiyankheni, Yehova; mzimu wanga ukutha. Musandibisire nkhope yanu; ndingafanane nao akutsikira kudzenje.


Yehova, imvani chilungamo, mverani mfuu wanga; tcherani khutu ku pemphero langa losatuluka m'milomo ya chinyengo.


Musandibisire ine nkhope yanu; musachotse kapolo wanu ndi kukwiya. Inu munakhala thandizo langa; musanditaye, ndipo musandisiye Mulungu wa chipulumutso changa.


Kwa Inu, Yehova, ndidzafuulira; thanthwe langa, musandikhalire ngati wosamva; pakuti ngati munditontholera ine, ndidzafanana nao iwo akutsikira kumanda.


Mverani mau anga, Yehova, Zindikirani kulingirira kwanga.


Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu, ndipo musandilange muukali wanu.


Imvani mfuu wanga, Mulungu; mverani pemphero langa.


Imvani Mulungu, mau anga, m'kudandaula kwanga; sungani moyo wanga angandiopse mdani.


Mbusa wa Israele, tcherani khutu; inu wakutsogolera Yosefe ngati nkhosa; inu wokhala pa akerubi, walitsani.


Yehova, Mulungu wa makamu, mudzakwiyira pemphero la anthu anu kufikira liti?


Yehova Mulungu wa makamu, imvani pemphero langa. Tcherani khutu, Mulungu wa Yakobo.


Tcherani khutu pemphero langa, Yehova; nimumvere mau a kupemba kwanga.


munamva mau anga; musabise khutu lanu popuma ndi pofuula ine.


Inde, pofuula ine ndi kuitana andithandize amakaniza pemphero langa.


Pakuti maso a Ambuye ali pa olungama, ndi makutu ake akumva pembedzo lao; koma nkhope ya Ambuye ili pa ochita zoipa.