Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 49:6 - Buku Lopatulika

Iwo akutama kulemera kwao; nadzitamandira pa kuchuluka kwa chuma chao;

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Iwo akutama kulemera kwao; nadzitamandira pa kuchuluka kwa chuma chao;

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Anthu otero amangokhulupirira chuma chao, amanyada chifukwa ali ndi chuma chambiri.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Iwo amene adalira kulemera kwawo ndi kutamandira kuchuluka kwa chuma chawo?

Onani mutuwo



Masalimo 49:6
17 Mawu Ofanana  

Nawawerengera Hamani kulemera kwake kwakukulu, ndi ana ake ochuluka, ndi zonse mfumu idamkuza nazo, ndi umo adamkweza koposa akalonga ndi anyamata a mfumu.


Sadzaopa mbiri yoipa; mtima wake ngwokhazikika, wokhulupirira Yehova.


Mtima wake ngwochirikizika, sadzachita mantha, kufikira ataona chofuna iye pa iwo omsautsa.


Tapenyani, suyu munthuyu amene sanamuyese Mulungu mphamvu yake; amene anatama kuchuluka kwa chuma chake, nadzilimbitsa m'kuipsa kwake.


Tsiku lonse atenderuza mau anga, zolingirira zao zonse zili pa ine kundichitira choipa.


Kodi adzapulumuka ndi zopanda pake? Gwetsani anthu mumkwiyo, Mulungu.


Musakhulupirire kusautsa, ndipo musatama chifwamba; chikachuluka chuma musakhazikepo mitima yanu.


Chuma cha wolemera ndi mzinda wake wolimba; koma umphawi wao uononga osauka.


Wokhulupirira chuma chake adzagwa; koma olungama adzaphuka ngati tsamba.


Kodi upenyeranji chimene kulibe? Pakuti chuma chimera mapiko, ngati mphungu youluka mumlengalenga.


Atero Yehova, wanzeru asadzitamandire m'nzeru zake, wamphamvu asadzitamandire m'mphamvu yake, wachuma asadzitamandire m'chuma chake;


Ndipo Efuremu anati, Zedi ndasanduka wolemera, ndadzionera chuma m'ntchito zonse ndinazigwira; sadzapeza mwa ine mphulupulu yokhala tchimo.


Ndipo ophunzirawo anazizwa ndithu ndi mau ake. Koma Yesu anayankhanso nanena nao, Ananu, nkovuta ndithu kwa iwo akutama chuma kulowa mu Ufumu wa Mulungu!


Ndipo ndidzati kwa moyo wanga, Moyo iwe, uli nacho chuma chambiri chosungika kufikira zaka zambiri; tapumulatu, nudye, numwe, nukondwere.


Lamulira iwo achuma m'nthawi ino ya pansi pano, kuti asadzikuze, kapena asayembekezere chuma chosadziwika kukhala kwake, koma Mulungu, amene atipatsa ife zonse kochulukira, kuti tikondwere nazo;