Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 49:4 - Buku Lopatulika

Ndidzatchera khutu kufanizo, ndidzafotokozera chophiphiritsa changa poimbira.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndidzatchera khutu kufanizo, ndidzafotokozera chophiphiritsa changa poimbira.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ndidzakupherani mwambi, ndidzamasulira tanthauzo lake poimba pangwe.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndidzatchera khutu langa ku mwambo, ndi pangwe ndidzafotokoza momveka mwambi wanga.

Onani mutuwo



Masalimo 49:4
10 Mawu Ofanana  

Ndidzatsegula pakamwa panga mofanizira; ndidzatchula zinsinsi zoyambira kale.


kuzindikira mwambi ndi tanthauzo lake, mau a anzeru, ndi zophiphiritsa zao.


Pamenepo ndinati, Ha, Ambuye Yehova! Anandinena, Wonena mafanizo uyu.


Ndipo potsiriza pake pa ufumu wao, atakwanira olakwa, idzauka mfumu ya nkhope yaukali yakuzindikira zinsinsi.


Ndimanena naye pakamwa ndi pakamwa, moonekera, osati mophiphiritsa; ndipo amapenyerera maonekedwe a Yehova; potero munalekeranji kuopa kutsutsana naye mtumiki wanga, Mose.


Ndipo ananena fanizo lake, nati, Ku Aramu ananditenga Balaki, mfumu ya Mowabu ananditenga ku mapiri a kum'mawa, Idza, udzanditembererere Yakobo. Idza, nudzanyoze Israele.


kuti chikachitidwe chonenedwa ndi mneneri, kuti, Ndidzatsegula pakamwa panga ndi mafanizo; ndidzawulula zinthu zobisika chiyambire kukhazikidwa kwake kwa dziko lapansi.


Chifukwa chake zonse zimene mwazinena mumdima zidzamveka poyera; ndipo chimene mwalankhula m'khutu, m'zipinda za m'kati chidzalalikidwa pa matsindwi a nyumba.


Pokhala nacho tsono chiyembekezo chotere, tilankhula ndi kukhazikika mtima kwakukulu,