Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 48:7 - Buku Lopatulika

Muswa zombo za ku Tarisisi ndi mphepo ya kum'mawa.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Muswa zombo za ku Tarisisi ndi mphepo ya kum'mawa.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Inu Mulungu mudaŵaononga, monga momwe mphepo yakuvuma ija imapasulira zombo zopita ku Tarisisi.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Inu munawawononga monga sitima zapamadzi za ku Tarisisi zitawonongeka ndi mphepo ya kummawa.

Onani mutuwo



Masalimo 48:7
7 Mawu Ofanana  

Popeza mfumu inali nazo panyanja zombo za ku Tarisisi, pamodzi ndi zombo za Hiramu; zombo za ku Tarisisi zinafika kamodzi zitapita zaka zitatu, zili nazo golide, ndi siliva, ndi minyanga, ndi apusi, ndi mbalame za zitsukwa zazitali za mawangamawanga.


Yehosafati anamanga zombo za ku Tarisisi kukatenga golide ku Ofiri; koma sizinamuke, popeza zinaphwanyika pa Eziyoni-Gebere.


Mitundu ya anthu idamva, inanthunthumira; kuda mtima kwagwira anthu okhala mu Filistiya.


ndipo adzaopa; zowawa ndi masauko zidzawagwira; ndipo adzamva zowawa, ngati mkazi wakubala; adzazizwa wina ndi wina; nkhope zao zidzanga malawi a moto.


ndi pa ngalawa zonse za Tarisisi, ndi pa zithunzithunzi zonse zokondweretsa.


Ndidzamwazamwaza iwo monga ndi mphepo ya kum'mawa pamaso pa adani; ndidzayang'anira pamsana pao, si nkhope yao, tsiku la Tsoka lao.