Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 48:6 - Buku Lopatulika

Pomwepo anagwidwa nako kunthunthumira; anamva chowawa, ngati wam'chikuta.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Pomwepo anagwidwa nako kunthunthumira; anamva chowawa, ngati wam'chikuta.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Adanjenjemera koopsa, ndipo adamva ululu wonga wa mkazi wovutika pa nthaŵi yochira.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Pomwepo anagwidwa nako kunjenjemera, ululu wonga wa mkazi woyembekezera pa nthawi yochira.

Onani mutuwo



Masalimo 48:6
7 Mawu Ofanana  

Nanyamuka, nathawa kuli sisiro, nasiya mahema ao, ndi akavalo ao, ndi abulu ao, misasa ili chimangire; nathawa apulumutse moyo wao.


Chifukwa chake m'chuuno mwanga mwadzazidwa ndi zopota; zopweteka zandigwira ine monga zopweteka za mkazi pobala mwana; zowawa zindiweramitsa, makutu anga sangathe kumva; ndichita mantha sindingathe kuona.


Pamenepo padasandulika pa nkhope pake pa mfumu, ndi maganizo ake anamsautsa, ndi mfundo za m'chuuno mwake zinaguluka, ndi maondo ake anaombana.


Zowawa zonga za mkazi wobala zidzamgwera, ndiye mwana wopanda nzeru; pakuti pali nyengo yakuti asachedwe mobalira ana.