Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 45:12 - Buku Lopatulika

Ndipo mwana wamkazi wa Tiro adzafika nayo mphatso; achuma a mwa anthu adzapempha kudziwika nanu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo mwana wamkazi wa Tiro adzafika nayo mphatso; achuma a mwa anthu adzapempha kudziwika nanu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Anthu a ku Tiro adzakukopa ndi mphatso, olemera kwambiri adzakunyengerera

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mwana wa mkazi wa ku Turo adzabwera ndi mphatso, amuna a chuma adzafunafuna kukoma mtima kwako.

Onani mutuwo



Masalimo 45:12
12 Mawu Ofanana  

Onenepa onse a padziko lapansi adzadya nadzagwadira; onse akutsikira kufumbi adzawerama pamaso pake, ndi iye amene sadziwa kusunga moyo wake.


Chifukwa cha Kachisi wanu wa mu Yerusalemu mafumu adzabwera nacho chaufulu kukupatsani.


Mafumu a ku Tarisisi ndi ku Zisumbuzo adzabwera nacho chopereka; mafumu a ku Sheba ndi Seba adzadza nazo mphatso.


Nkhunda yangawe, yokhala m'ming'alu ya thanthwe, mobisika motsetsereka, ndipenye nkhope yako, ndimve mau ako; pakuti mau ako ngokoma, nkhope yako ndi kukongola.


Tiye, bwenzi langa, tinke kuminda; titsotse m'midzi.


Ndipo mafumu adzakulera, ndi akazi ao aakulu adzakuyamwitsa; iwo adzakugwadira ndi nkhope zao zoyang'ana pansi, nadzaseteka fumbi la m'mapazi ako: ndipo iwe udzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndi iwo amene alindira Ine sadzakhala ndi manyazi.


Ndipo amitundu adzafika kwa kuunika kwako, ndi mafumu kwa kuyera kwa kutuluka kwako.


Ndipo pofika kunyumba anaona kamwanako ndi Maria amake, ndipo anagwa pansi namgwadira Iye; namasula chuma chao, nampatsa Iye mitulo, ndiyo golide ndi lubani ndi mure.