Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 44:9 - Buku Lopatulika

Koma mwatitaya, ndi kutinyazitsa; ndipo simutuluka nao makamu a nkhondo athu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Koma mwatitaya, ndi kutinyazitsa; ndipo simutuluka nao makamu a nkhondo athu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Komabe Inu mwatitaya, ndipo mwatitsitsa, simunapite nawo limodzi ankhondo athu.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa; Inu simupitanso ndi ankhondo athu.

Onani mutuwo



Masalimo 44:9
13 Mawu Ofanana  

Si ndinu Mulungu, amene mwatitaya osatuluka nao magulu athu?


Pakuti Inu ndinu Mulungu wa mphamvu yanga; mwanditayiranji? Ndimayenderanji woliralira chifukwa cha kundipsinja mdani?


Mwatitaya Mulungu, mwatipasula; mwakwiya; tibwezereni.


Si ndinu, Mulungu, amene mwatitaya? Osatuluka nao makamu athu, Mulungu.


Mulungu, munatitayiranji chitayire? Mkwiyo wanu ufukiranji pa nkhosa za kubusa kwanu?


Yehova mutayiranji moyo wanga? Ndi kundibisira nkhope yanu?


Atero Yehova, wanzeru asadzitamandire m'nzeru zake, wamphamvu asadzitamandire m'mphamvu yake, wachuma asadzitamandire m'chuma chake;


koma wakudzitamandira adzitamandire adzikweze umo, kuti ali wakuzindikira, ndi kundidziwa Ine, kuti ndine Yehova wakuchita zokoma mtima, chiweruziro, ndi chilungamo m'dziko lapansi, pakuti m'menemo ndikondwerera, ati Yehova.