Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 41:10 - Buku Lopatulika

Koma Inu, Yehova, mundichitire chifundo, ndipo mundiutse, kuti ndiwabwezere.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Koma Inu, Yehova, mundichitire chifundo, ndipo mundiutse, kuti ndiwabwezere.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Koma Inu Chauta, mundikomere mtima, mundichiritse kuti ndiŵalange anthuwo.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Koma Yehova mundichititre chifundo, dzutseni kuti ndiwabwezere.

Onani mutuwo



Masalimo 41:10
13 Mawu Ofanana  

Ndipo Abisalomu anaitana Ahitofele Mgiloni, phungu wa Davide, kumzinda wake ndiwo Gilo, pamene iye analikupereka nsembe. Ndipo chiwembucho chinali cholimba; pakuti anthu anachulukachulukabe kwa Abisalomu.


mabwenzi anga enieni onse anyansidwa nane; ndi onse ndakondana nao asandulika adani anga.


Ndipo Inu Yehova, ndinu chikopa changa; ulemerero wanga, ndi wondiweramutsa mutu wanga.


Koma ameneyo ndiwe, munthu woyenerana nane, tsamwali wanga, wodziwana nane.


Tinapangirana upo wokoma, tinaperekeza khamu la anthu popita kunyumba ya Mulungu.


Mundichitire chifundo, Mulungu, mundichitire chifundo; pakuti moyo wanga ukhulupirira Inu, ndipo ndithawira kumthunzi wa mapiko anu, kufikira zosakazazo zidzapita.


Pakuti ndamva kugogodera kwa ambiri, mantha pozungulira ponse. Neneza, ndipo tidzamneneza iye, ati atsamwali anga onse, amene ayang'anira kutsimphina kwanga; kapena adzakopedwa, ndipo ife tidzampambana iye, ndipo tidzambwezera chilango.


Anthu onse a akupangana nawe anakuperekeza mpaka pamalire; anthu okhala ndi mtendere nawe anakunyenga, nakuposa mphamvu; iwo akudya chakudya chako akutchera msampha pansi pako; mulibe nzeru mwa iye.


Koma adani anga aja osafuna kuti ndidzakhala mfumu yao, bwerani nao kuno, nimuwaphe pamaso panga.