Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 39:8 - Buku Lopatulika

Ndipulumutseni kwa zolakwa zanga zonse, musandiike ndikhale chotonza cha wopusa.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipulumutseni kwa zolakwa zanga zonse, musandiike ndikhale chotonza cha wopusa.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pulumutseni ku zolakwa zanga zonse. Musandisandutse chinthu chochinyodola zitsiru.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Pulumutseni ku zolakwa zanga zonse; musandisandutse chonyozeka kwa opusa.

Onani mutuwo



Masalimo 39:8
19 Mawu Ofanana  

Mundipatutsire chotonza changa ndichiopacho; popeza maweruzo anu ndi okoma.


Moyo wanga uyang'anira Ambuye, koposa alonda matanda kucha; inde koposa alonda matanda kucha.


Ndipo adzaombola Israele ku mphulupulu zake zonse.


Chifukwa cha dzina lanu, Yehova, ndikhululukireni kusakaza kwanga, pakuti ndiko kwakukulu.


Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga; ndipo khululukirani zolakwa zanga zonse.


Ndipo andiyasamira m'kamwa mwao; nati, Hede, Hede, diso lathu lidachipenya.


Mutisandutsa chotonza kwa anzathu, ndi choseketsa ndi cholalatitsa iwo akutizinga.


Mundilanditse kumlandu wa mwazi, Mulungu, ndinu Mulungu wa chipulumutso changa; lilime langa lidzakweza nyimbo ya chilungamo chanu.


Adzanditumizira m'mwamba, nadzandipulumutsa ponditonza wofuna kundimeza; Mulungu adzatumiza chifundo chake ndi choonadi chake.


Mphulupulu zinandipambana; koma mudzafafaniza zolakwa zathu.


Takhala chotonza cha anansi athu, ndi choseketsa ndi cholalatitsa iwo akutizinga.


Ansembe, atumiki a Yehova, alire pakati pa khonde la pakhomo ndi guwa la nsembe, nanene, Alekeni anthu anu, Yehova, musapereka cholowa chanu achitonze, kuti amitundu awalamulire; adzaneneranji mwa anthu, Ali kuti Mulungu wao?


Ndipo Yehova anayankha, nati kwa anthu ake, Taonani, ndidzakutumizirani tirigu, ndi vinyo, ndi mafuta; ndipo mudzakhuta ndi izo; ndipo sindidzakuperekaninso mukhale chitonzo mwa amitundu;


Adzabwera, nadzatichitira nsoni; adzagonjetsa mphulupulu zathu; ndipo mudzataya zochimwa zao zonse m'nyanja yakuya.


Ndipo adzabala mwana wamwamuna, ndipo udzamutcha dzina lake Yesu; pakuti Iyeyo adzapulumutsa anthu ake kumachimo ao.


amene anadzipereka yekha m'malo mwa ife, kuti akatiombole ife kuzoipa zonse, nakadziyeretsere yekha anthu akhale ake enieni, achangu pa ntchito zokoma.