Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 38:6 - Buku Lopatulika

Ndapindika, ndawerama kwakukulu; ndimayenda woliralira tsiku lonse.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndapindika, ndawerama kwakukulu; ndimayenda woliralira tsiku lonse.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ndapindika msana kwathunthu, ndaŵerama zedi, ndatha mphamvu, tsiku lonse ndimangonka ndilira.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ine ndapindika msana ndipo ndawerama kwambiri; tsiku lonse ndimangolira.

Onani mutuwo



Masalimo 38:6
13 Mawu Ofanana  

Ndiyenda ndili wothimbirira osati ndi dzuwa ai; ndinyamuka mumsonkhano ndi kufuula.


Mnofu wanga wavala mphutsi ndi nkanambo zadothi; khungu langa lang'ambika, nilinyansa.


Anthu opusa azunzika chifukwa cha zolakwa zao, ndi chifukwa cha mphulupulu zao.


Yehova agwiriziza onse akugwa, naongoletsa onse owerama.


Pakuti moyo wanga watha ndi chisoni, ndi zaka zanga zatha ndi kuusa moyo. Mphamvu yanga yafooka chifukwa cha kusakaza kwanga, ndi mafupa anga apuwala.


Ndakhala ine monga ngati iye anali bwenzi langa, kapena mbale wanga; polira ndinaweramira pansi, monga munthu wakulira maliro amai wake.


Udziweramiranji moyo wanga iwe? Ndi kuzingwa m'kati mwanga? Yembekeza Mulungu, pakuti ndidzamyamikanso chifukwa cha chipulumutso cha nkhope yake.


Ndidzati kwa Mulungu, thanthwe langa, mwandiiwala chifukwa ninji? Ndimayenderanji wakulira chifukwa cha kundipsinja mdaniyo?


Pakuti Inu ndinu Mulungu wa mphamvu yanga; mwanditayiranji? Ndimayenderanji woliralira chifukwa cha kundipsinja mdani?


Ananditchera ukonde apo ndiyenda; moyo wanga wawerama. Anandikumbira mbuna patsogolo panga; anagwa m'kati mwake iwo okha.


Ndalema nako kuusa moyo kwanga; ndiyandamitsa kama wanga usiku wonse; mphasa yanga ndiolobza ndi misozi yanga.


Diso langa lapuwala chifukwa cha kuzunzika kwanga: Ndimaitana Inu, Yehova, tsiku lonse; nditambalitsira manja anga kwa Inu.


Ndinalankhulalankhula ngati namzeze, pena chumba; Ndinalira maliro ngati nkhunda; maso anga analephera pogadamira kumwamba. Ambuye ndasautsidwa, mundiperekere chikoli.