Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 34:9 - Buku Lopatulika

Opani Yehova, inu oyera mtima ake; chifukwa iwo akumuopa Iye sasowa.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Opani Yehova, inu oyera mtima ake; chifukwa iwo akumuopa Iye sasowa.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Muzimvera Chauta, inu anthu ake oyera mtima, pakuti amene amamumvera sasoŵa kanthu.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Wopani Yehova inu oyera mtima ake, pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.

Onani mutuwo



Masalimo 34:9
13 Mawu Ofanana  

Ndipo mthenga anati, Usaike dzanja lako pa mwana, usamchitire iye kanthu; chifukwa tsopano ndidziwa kuti iwe umuopa Mulungu wako, pakuti sunandikanize ine mwana wako, mwana wako wayekha.


Mpsompsoneni Mwanayo, kuti angakwiye, ndipo mungatayike m'njira ukayaka pang'ono pokha mkwiyo wake. Odala onse akumkhulupirira Iye.


Inu akuopa Yehova, mumlemekeze; inu nonse mbumba ya Yakobo, mumchitire ulemu; ndipo muchite mantha ndi Iye, inu nonse mbumba ya Israele.


Yehova ndiye mbusa wanga; sindidzasowa.


Kondani Yehova, Inu nonse okondedwa ake, Yehova asunga okhulupirika, ndipo abwezera zochuluka iye wakuchita zodzitama.


Ndiye Mulungu, ayenera kumuopa kwambiri mu upo wa oyera mtima, ndiye wochititsa mantha koposa onse akumzinga.


atatero ana a Israele adzabwera, nadzafuna Yehova Mulungu wao, ndi Davide mfumu yao, nadzafika ndi mantha kwa Yehova, ndi ku ukoma wake masiku otsiriza.


Iye amene sanatimane Mwana wake wa Iye yekha, koma anampereka chifukwa cha ife tonse, adzalekeranji kutipatsanso ife zinthu zonse kwaulere pamodzi ndi Iye?


Koma Mulungu wanga adzakwaniritsa chosowa chanu chilichonse monga mwa chuma chake mu ulemerero mwa Khristu Yesu.