Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 30:9 - Buku Lopatulika

M'mwazi mwanga muli phindu lanji, potsikira ine kudzenje? Ngati fumbi lidzayamika Inu? Ngati lidzalalikira choonadi chanu?

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

M'mwazi mwanga muli phindu lanji, potsikira ine kudzenje? Ngati fumbi lidzayamika Inu? Ngati lidzalalikira choonadi chanu?

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

“Kodi mudzapindulanji pa imfa yanga ngati nditsikira ku manda? Kodi ine nditasanduka fumbi, ndingathe kukutamandani? Kodi pamenepo ndingathe kulalika za kukhulupirika kwanu?

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

“Kodi pali phindu lanji powonongeka kwanga ngati nditsikira ku dzenje? Kodi fumbi lidzakutamandani Inu? Kodi lidzalengeza za kukhulupirika kwanu?

Onani mutuwo



Masalimo 30:9
7 Mawu Ofanana  

Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo, ndipo ndidzafotokozera ntchito za Yehova.


Pakuti muimfa m'mosakumbukira Inu; m'mandamo adzakuyamikani ndani?


Ndinamfuulira Iye pakamwa panga, ndipo ndinamkuza ndi lilime langa.


Chilichonse dzanja lako lichipeza kuchichita, uchichite ndi mphamvu yako; pakuti mulibe ntchito ngakhale kulingirira ngakhale kudziwa, ngakhale nzeru, kumanda ulikupitako.


Pakuti kunsi kwa manda sikungakuyamikeni Inu; imfa singakulemekezeni; Otsikira kudzenje sangaziyembekeze zoona zanu.