Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 30:3 - Buku Lopatulika

Yehova munabweza moyo wanga kumanda, munandisunga ndi moyo, kuti ndingatsikire kudzenje.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Yehova munabweza moyo wanga kumanda, munandisunga ndi moyo, kuti ndingatsikire kudzenje.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Inu Chauta, mwanditulutsa m'dziko la akufa, mwandibwezeranso moyo kuti ndingatsikire ku manda.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Inu Yehova, munanditulutsa ku manda, munandisunga kuti ndisatsalire mʼdzenje.

Onani mutuwo



Masalimo 30:3
13 Mawu Ofanana  

Koma anandiombola ndingatsikire kumanda, ndi moyo wanga udzaona kuunika.


Atumiza mau ake nawachiritsa, nawapulumutsa ku chionongeko chao.


Pakuti munalanditsa moyo wanga kuimfa, maso anga kumisozi, mapazi anga, ndingagwe.


Pakuti simudzasiya moyo wanga kumanda; simudzalola wokondedwa wanu avunde.


Kwa Inu, Yehova, ndidzafuulira; thanthwe langa, musandikhalire ngati wosamva; pakuti ngati munditontholera ine, ndidzafanana nao iwo akutsikira kumanda.


Pakuti mwalanditsa moyo wanga kuimfa, simunatero nao mapazi anga kuti ndingagwe? Kuti ndiyende pamaso pa Mulungu m'kuunika kwa amoyo.


Inu, amene munationetsa nsautso zambiri ndi zoipa, mudzatipatsanso moyo, ndi kutitenganso munsi mwa dziko.


Pakuti chifundo chanu cha pa ine nchachikulu; ndipo munalanditsa moyo wanga kunsi kwa manda.


Ambuye ndi zinthu izi anthu akhala ndi moyo. Ndipo m'menemo monse muli moyo wa mzimu wanga; Chifukwa chake mundichiritse ine, ndi kundikhalitsa ndi moyo.