Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 30:2 - Buku Lopatulika

Yehova, Mulungu wanga, ndinafuulira kwa Inu, ndipo munandichiritsa.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Yehova, Mulungu wanga, ndinafuulira kwa Inu, ndipo munandichiritsa.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Chauta, Mulungu wanga, ndidalirira Inu kuti mundithandize, ndipo mwandichiritsa.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Inu Yehova Mulungu wanga ndinapempha kwa Inu thandizo ndipo Inu munandichiritsa.

Onani mutuwo



Masalimo 30:2
14 Mawu Ofanana  

Ndipo Abrahamu anapemphera Mulungu, ndipo Mulungu anachiritsa Abimeleki, ndi mkazi wake, ndi adzakazi ake; ndipo anabala ana.


Bwerera, nunene kwa Hezekiya mtsogoleri wa anthu anga, Atero Yehova Mulungu wa Davide kholo lako, Ndamva pemphero lako, ndapenya misozi yako; taona, ndidzakuchiritsa, tsiku lachitatu udzakwera kunka kunyumba ya Yehova.


Kulanga anandilangadi Yehova: koma sanandipereke kuimfa ai.


Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu; ndipo ndidzalemekeza dzina lanu kunthawi za nthawi.


Achiritsa osweka mtima, namanga mabala ao.


Mundiweruze monga mwa chilungamo chanu, Yehova Mulungu wanga; ndipo asandisekerere ine.


Ndipo ine, mundigwirizize mu ungwiro wanga, ndipo mundiike pankhope panu kunthawi yamuyaya.


Mundimvetse chimwemwe ndi kusekera, kuti mafupawo munawathyola akondwere.


Mundichitire chifundo, Yehova; pakuti ndalefuka ine. Mundichize, Yehova; pakuti anthunthumira mafupa anga.


Koma ndinafuulira kwa Inu, Yehova, ndipo pemphero langa lifika kwa Inu mamawa.


ndipo anati, Ngati udzamveratu mau a Yehova, Mulungu wako, ndi kuchita zoona pamaso pake, ndi kutchera khutu pa malamulo ake, ndi kusunga malemba ake onse, za nthenda zonse ndinaziika pa Aejipito sindidzaziika pa iwe nnena imodzi; pakuti Ine Yehova ndine wakuchiritsa iwe.