Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 27:10 - Buku Lopatulika

Pakuti wandisiya atate wanga ndi amai wanga, koma Yehova anditola.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Pakuti wandisiya atate wanga ndi amai wanga, koma Yehova anditola.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ngakhale bambo wanga ndi mai wanga andisiye ndekha, Inu Chauta mudzandisamala.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ngakhale abambo ndi amayi anga anditaya Yehova adzandisamala.

Onani mutuwo



Masalimo 27:10
9 Mawu Ofanana  

Ndipo Davide ananena ndi Abisai ndi anyamata ake onse, Onani, mwana wanga wotuluka m'matumbo anga, alikufuna moyo wanga; koposa kotani nanga Mbenjamini uyu? Mlekeni, atukwane, pakuti Yehova anamuuza.


Abale anga andiyesa mlendo, ndi ana a mai wanga andiyesa wa mtundu wina.


Iye adzadyetsa zoweta zake ngati mbusa, nadzasonkhanitsa anaankhosa m'manja mwake, nadzawatengera pa chifuwa chake, ndipo adzatsogolera bwinobwino zimene ziyamwitsa.


Kodi mkazi angaiwale mwana wake wa pabere, kuti iye sangachitire chifundo mwana wombala iye? Inde awa angaiwale, koma Ine sindingaiwale iwe.


ndipo apabanja ake a munthu adzakhala adani ake.


Onani ikudza nthawi, ndipo yafika, imene mudzabalalitsidwa, yense ku zake za yekha, ndipo mudzandisiya Ine pa ndekha. Ndipo sindikhala pa ndekha, chifukwa Atate ali pamodzi ndi Ine,


Yesu anamva kuti adamtaya kunja; ndipo pakumpeza iye, anati, Kodi ukhulupirira Mwana wa Munthu?


Pa chodzikanira changa choyamba panalibe mmodzi anandithangata, koma onse anandisiya; chimenecho chisawerengedwe chowatsutsa.