Masalimo 24:6 - Buku Lopatulika Uwu ndi mbadwo wa iwo akufuna Iye, iwo akufuna nkhope yanu, Mulungu wa Yakobo. Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 Uwu ndi mbadwo wa iwo akufuna Iye, iwo akufuna nkhope yanu, Mulungu wa Yakobo. Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa Anthu otere ndiwo amene amafunitsitsa Chauta, ndiwo amene amabwera kudzapembedza Mulungu wa Yakobe. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Umenewo ndiwo mʼbado wa amene amafunafuna Yehova; amene amafunafuna nkhope yanu, Inu Mulungu wa Yakobo. Sela |
Pamene munati, Funani nkhope yanga; mtima wanga unati kwa Inu. Nkhope yanu, Yehova, ndidzaifuna.
ndikadati, Ndidzafotokozera chotere, taonani, ndikadachita chosakhulupirika ndi mbadwo wa ana ako.
Koma kunakomera Yehova kumtundudza; anammvetsa zowawa; moyo wake ukapereka nsembe yopalamula, Iye adzaona mbeu yake, adzatanimphitsa masiku ake; ndipo chomkondweretsa Yehova chidzakula m'manja mwake.
Yesu anaona Natanaele alinkudza kwa Iye, nanena za iye, Onani, Mwisraele ndithu, mwa iye mulibe chinyengo!
Chifukwa chake chilungamo chichokera m'chikhulupiriro, kuti chikhale monga mwa chisomo; kuti lonjezo likhale lokhazikika kwa mbeu zonse; si kwa iwo a chilamulo okhaokha, koma kwa iwonso a chikhulupiriro cha Abrahamu; ndiye kholo la ife tonse;
Koma inu ndinu mbadwa yosankhika, ansembe achifumu, mtundu woyera mtima, anthu a mwini wake, kotero kuti mukalalikire zoposazo za Iye amene anakuitanani mutuluke mumdima, mulowe kuunika kwake kodabwitsa;