Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 22:11 - Buku Lopatulika

Musandikhalire kutali; pakuti nsautso ili pafupi, pakuti palibe mthandizi.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Musandikhalire kutali; pakuti nsautso ili pafupi, pakuti palibe mthandizi.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Musandikhalire kutali, pakuti mavuto ali pafupi kundigwera, ndipo palibe wina wondithandiza.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Musakhale kutali ndi ine, pakuti mavuto ali pafupi ndipo palibe wina wondipulumutsa.

Onani mutuwo



Masalimo 22:11
18 Mawu Ofanana  

Pakuti Yehova anapenya kuti kuzunzika kwao kwa Israele nkowawa ndithu; popeza panalibe womangika kapena womasuka, ndipo panalibe womthandiza Israele.


Muimiranji patali, Yehova? Mubisaliranji m'nyengo za nsautso?


Yehova, mudazipenya; musakhale chete, Ambuye, musakhale kutali ndi ine.


Musanditaye, Yehova, Mulungu wanga, musakhale kutali ndi ine.


Yandikizani moyo wanga, ndi kuuombola; ndipulumutseni chifukwa cha adani anga.


Musandikhalire kutali, Mulungu; fulumirani kundithandiza, Mulungu.


Inu munandigwiriziza kuyambira ndisanabadwe, kuyambira pa thupi la mai wanga wondichitira zokoma ndinu; ndidzakulemekezani kosalekeza.


Pakuti adzapulumutsa waumphawi wofuulayo; ndi wozunzika amene alibe mthandizi.


Ndipo ndinayang'ana, koma panalibe wothangata; ndipo ndinadabwa kuti panalibe wochirikiza; chifukwa chake mkono wangawanga unanditengera chipulumutso, ndi ukali wanga unandichirikiza Ine.


Koma izi zonse zinachitidwa, kuti zolembedwa za aneneri zikwaniridwe. Pomwepo ophunzira onse anamsiya Iye, nathawa.


Ndipo anakananso ndi chilumbiro, kuti, Sindidziwa munthuyo.


Pamenepo iye anayamba kutemberera ndi kulumbira, kuti, Sindidziwa munthuyo. Ndipo pompo tambala analira.


Onani ikudza nthawi, ndipo yafika, imene mudzabalalitsidwa, yense ku zake za yekha, ndipo mudzandisiya Ine pa ndekha. Ndipo sindikhala pa ndekha, chifukwa Atate ali pamodzi ndi Ine,


Popeza Yehova adzaweruza anthu ake, nadzachitira nsoni anthu ake; pakuona Iye kuti mphamvu yao yatha, wosatsala womangika kapena waufulu.


Ameneyo, m'masiku a thupi lake anapereka mapemphero ndi mapembedzero pamodzi ndi kulira kwakukulu ndi misozi kwa Iye amene anakhoza kumpulumutsa Iye muimfa, ndipo anamveka popeza anaopa Mulungu,