Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 21:11 - Buku Lopatulika

Pakuti anakupangirani choipa, anapangana chiwembu, osakhoza kuchichita.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Pakuti anakupangirani choipa, anapangana chiwembu, osakhoza kuchichita.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Akafuna kuti aichite choipa ndi kuipweteka, adzalephereratu,

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ngakhale iwo akukonzereni chiwembu mwa kuchenjera kwawo sadzapambana;

Onani mutuwo



Masalimo 21:11
18 Mawu Ofanana  

Podzikuza woipa apsereza waumphawi; agwe m'chiwembu anapanganacho.


Zidzukulu zake zidulidwe; dzina lao lifafanizidwe mu mbadwo ukudza.


Aphokoseranji amitundu, nalingiriranji anthu zopanda pake?


Pakuti ndamva ugogodi wa ambiri, mantha andizinga. Pondipangira chiwembu, anatsimikiza mtima kulanda moyo wanga.


Pakuti salankhula zamtendere, koma apangira chiwembu odekha m'dziko.


Amati, Tiyeni tiwaononge asakhalenso mtundu wa anthu; ndipo dzina la Israele lisakumbukikenso.


Ndipo anati kwa ine, Wobadwa ndi munthu iwe, awa ndi anthu olingirira za mphulupulu, ndi kupangira uphungu woipa m'mzinda muno;


Pamenepo Herode, poona kuti anampusitsa Anzeruwo, anapsa mtima ndithu, natumiza ena kukaononga tiana tonse ta mu Betelehemu ndi ta m'midzi yake yonse, takufikira zaka ziwiri ndi tating'ono tonse, monga mwa nthawi imeneyo iye anafunsitsa kwa Anzeruwo.


Nawatumiza ku Betelehemu, nati, Yendani mufunitsitse za kamwanako; ndipo pamene mudzampeza, mundibwezere mau, kuti inenso ndidzadze kudzamlambira Iye.


Ndipo pamene anafuna kumgwira, anaopa makamu a anthu, chifukwa anamuyesa mneneri.