Masalimo 19:5 - Buku Lopatulika ndipo lili ngati mkwati wakutuluka m'chipinda mwake, likondwera ngati chiphona kuthamanga m'njira. Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 ndipo lili ngati mkwati wakutuluka m'chipinda mwake, likondwera ngati chiphona kuthamanga m'njira. Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa Dzuŵalo limatuluka ngati mkwati wokondwa amene akutuluka m'nyumba mwake, ndipo limayenda ndi chimwemwe ngati ngwazi yamphamvu. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Dzuwa lili ngati mkwatibwi wobwera kuchokera ku nsanja yake, ngati katswiri wokondwerera kuthamanga pa mpikisano. |
Ndidzakondwa kwambiri mwa Yehova, moyo wanga udzakondwerera mwa Mulungu wanga; pakuti Iye wandiveka ine ndi zovala za chipulumutso, nandifunda chofunda cha chilungamo, monga mkwati avala nduwira, ndi monga mkwatibwi adzikometsa yekha ndi miyala yamtengo.
Pakuti monga mnyamata akwatira namwali, momwemo ana ako aamuna adzakukwatira iwe; ndi monga mkwati akondwera ndi mkwatibwi, momwemo Mulungu wako adzakondwera nawe.
Iye amene ali naye mkwatibwi ali mkwati, koma mnzake wa mkwatiyo, wakuimirira ndi kumvera iye, akondwera kwakukulu chifukwa cha mau a mkwatiyo; chifukwa chake chimwemwe changa chimene chakwanira.