Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 18:44 - Buku Lopatulika

Pakumva m'khutu za ine adzandimvera, alendo adzandigonjera monyenga.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Pakumva m'khutu za ine adzandimvera, alendo adzandigonjera monyenga.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Atangomva za ine adayamba kundimvera, anthu a maiko ena adabwera kwa ine kudzapemba.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine amandigonjera.

Onani mutuwo



Masalimo 18:44
9 Mawu Ofanana  

Ndipo Davide ananena ndi mnyamata wakumuuzayo, Kwanu nkuti? Nayankha, Ine ndine mwana wa mlendo, Mwamaleke.


Nenani kwa Mulungu, Ha, ntchito zanu nzoopsa nanga! Chifukwa cha mphamvu yanu yaikulu adani anu adzagonjera Inu.


Dzudzulani chilombo cha m'bango, khamu la mphongo ndi ng'ombe za anthu, yense wakudzigonjera ndi ndalama za siliva; anabalalitsa mitundu ya anthu ya kukondwera nayo nkhondo.


Akumuda Yehova akadamgonjera mungakhale monyenga, koma nyengo yao ikadakhala yosatha.


Yehova analumbira padzanja lake lamanja, ndi mkono wake wamphamvu, Zoonadi, sindidzaperekanso tirigu wako akhale chakudya cha adani ako, ndipo alendo sadzamwa vinyo wako amene iwe unagwirira ntchito;


popeza mwalowa nao achilendo osadulidwa m'mtima, osadulidwa m'thupi akhale m'malo anga opatulika kuwadetsa, ndiwo nyumba yanga, popereka inu mkate wanga, mafuta, ndi mwazi; ndipo munathyola pangano langa pamodzi ndi zonyansa zanu zonse.


Wodala iwe, Israele; akunga iwe ndani, mtundu wa anthu opulumutsidwa ndi Yehova, ndiye chikopa cha thandizo lako, Iye amene akhala lupanga la ukulu wako! Ndi adani ako adzakugonjera; ndipo udzaponda pa misanje yao.