Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 18:23 - Buku Lopatulika

Ndipo ndinakhala wangwiro ndi Iye, ndipo ndinadzisunga wosachita choipa changa.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo ndinakhala wangwiro ndi Iye, ndipo ndinadzisunga wosachita choipa changa.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ndinalibe mlandu pamaso pake, ndinkalewa zoipa m'moyo mwanga.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.

Onani mutuwo



Masalimo 18:23
9 Mawu Ofanana  

Ndidziwanso, Mulungu wanga, kuti muyesa mtima, nimukondwera nako kuongoka. Koma ine, ndi mtima wanga woongoka ndapereka zonsezi mwaufulu; ndipo tsopano ndaona mokondwera anthu anu okhala pompano, napereka kwa Inu mwaufulu.


Pakuti Yehova ndiye wolungama; akonda zolungama; woongoka mtima adzapenya nkhope yake.


Ndinasankha njira yokhulupirika; ndinaika maweruzo anu pamaso panga.


Mwayesera mtima wanga; mwandizonda usiku; mwandisuntha, simupeza kanthu; mwatsimikiza mtima kuti m'kamwa mwanga simudzalakwa.


Siyana nacho choipa, nuchite chokoma, nukhale nthawi zonse.


Ndipo Yehova adzabwezera munthu yense chilungamo chake ndi chikhulupiriko chake, popeza Yehova anakuperekani lero m'dzanja langa, koma sindinalole kutukulira dzanja langa pa wodzozedwa wa Yehova.