Nasonkhana pamodzi Ayuda ena okhala m'maiko a mfumu, nalimbikira moyo wao, napumula pa adani ao, nawapha a iwo odana nao zikwi makumi asanu ndi awiri mphambu zisanu; koma sanalande zofunkha.
Masalimo 149:7 - Buku Lopatulika kubwezera chilango akunja, ndi kulanga mitundu ya anthu; Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 kubwezera chilango akunja, ndi kulanga mitundu ya anthu; Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa kuti alipsire mafuko achikunja, kuti alange mitundu ina ya anthu. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero kubwezera chilango anthu a mitundu ina, ndi kulanga anthu a mitundu yonse, |
Nasonkhana pamodzi Ayuda ena okhala m'maiko a mfumu, nalimbikira moyo wao, napumula pa adani ao, nawapha a iwo odana nao zikwi makumi asanu ndi awiri mphambu zisanu; koma sanalande zofunkha.
ndiwo masiku amene Ayuda anapumula pa adani ao; ndi mwezi wachisoni unawasandulikira wakukondwera, ndi wamaliro ukhale tsiku lokoma, awayese masiku amadyerero ndi akukondwera, akutumizirana magawo, ndi akupatsa zaufulu kwa osauka.
Ndipo atatero, Yoswa anawakantha nawapha, nawapachika pa mitengo isanu; nalikupachikidwa pa mitengo mpaka madzulo.
Mutemberere Merozi, ati mthenga wa Yehova, mutemberere chitemberere nzika zake; pakuti sanadzathandize Yehova, kumthandiza Yehova pa achamuna.