Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 149:5 - Buku Lopatulika

Okondedwa ake atumphe mokondwera mu ulemu: Afuule mokondwera pamakama pao.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Okondedwa ake atumphe mokondwera m'ulemu: Afuule mokondwera pamakama pao.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Okhulupirika akondwerere chigonjetso chopambanachi, aziimba mokondwa ali gone pa mabedi.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Oyera mtima asangalale mu ulemu wake ndi kuyimba mwachimwemwe pa mabedi awo.

Onani mutuwo



Masalimo 149:5
12 Mawu Ofanana  

Chomwecho Davide ndi a nyumba yonse ya Israele anakwera nalo likasa la Yehova, ndi chimwemwe ndi kulira kwa malipenga.


Koma palibe anganene, Ali kuti Mulungu Mlengi wanga, wakupatsa nyimbo usiku;


M'mahema a olungama muli liu lakufuula mokondwera Dzanja lamanja la Yehova ndi la chipulumutso:


Ndipo ansembe ake ndidzawaveka ndi chipulumutso: Ndi okondedwa ake adzafuulitsa mokondwera.


Ntchito zanu zonse zidzakuyamikani, Yehova; ndi okondedwa anu adzakulemekezani.


Yehova ndiye mbusa wanga; sindidzasowa.


Koma usana Yehova adzalamulira chifundo chake, ndipo usiku nyimbo yake idzakhala ndi ine. Inde pemphero la kwa Mulungu wa moyo wanga.


Kuonetsera chifundo chanu mamawa, ndi chikhulupiriko chanu usiku uliwonse.


ndi mlandu unakomera opatulika a Wam'mwambamwamba, nifika nthawi yakuti ufumu unali wao wa opatulikawo.


amene ife tikhoza kulowa naye ndi chikhulupiriro m'chisomo ichi m'mene tilikuimamo; ndipo tikondwera m'chiyembekezo cha ulemerero wa Mulungu.


amene mungakhale simunamuone mumkonda; amene mungakhale simumpenya tsopano, pokhulupirira, mukondwera naye ndi chimwemwe chosaneneka, ndi cha ulemerero: