Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 143:6 - Buku Lopatulika

Nditambalitsira manja anga kwa Inu: Moyo wanga ulira Inu monga dziko lolira mvula.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Nditambalitsira manja anga kwa Inu: Moyo wanga ulira Inu monga dziko lolira mvula.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ndimatambalitsira manja anga kwa Inu, mtima wanga umamva ludzu lofuna Inu, monga limachitira dziko louma.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndatambalitsa manja anga kwa Inu; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu monga nthaka yowuma. Sela

Onani mutuwo



Masalimo 143:6
13 Mawu Ofanana  

Ukakonzeratu mtima wako, ndi kumtambasulira Iye manja ako;


Monga kapolo woliralira mthunzi, monga wolembedwa ntchito ayembekezera mphotho yake,


Misozi yanga yakhala ngati chakudya changa, usana ndi usiku; pakunena iwo kwa ine dzuwa lonse, Mulungu wako ali kuti?


Tikadaiwala dzina la Mulungu wathu, ndi kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo;


Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga; ndidzakufunani m'matanda kucha. Moyo wanga ukumva ludzu la kwa Inu, thupi langa lilirira Inu, m'dziko louma ndi lotopetsa, lopanda madzi.


Moyo wanga ulakalaka, inde ukomokanso ndi kufuna mabwalo a Yehova; mtima wanga ndi thupi langa zifuulira kwa Mulungu wamoyo.


Kodi mudzachitira akufa zodabwitsa? Kodi adzaukanso otisiyawo, ndi kukulemekezani?


Diso langa lapuwala chifukwa cha kuzunzika kwanga: Ndimaitana Inu, Yehova, tsiku lonse; nditambalitsira manja anga kwa Inu.


Ndipo Mose ananena naye, Potuluka m'mzinda ine, ndidzakweza manja anga kwa Yehova; mabingu adzaleka, ndi matalala sadzakhalaponso; kuti mudziwe kuti dziko lapansi nla Yehova.


Ndipo mchenga wong'azimira udzasanduka thamanda, ndi nthaka yopanda madzi idzasanduka zitsime zamadzi; m'malo a ankhandwe m'mene iwo anagona, mudzakhala udzu ndi mabango ndi milulu.


Koma tsiku lomaliza, lalikululo la chikondwerero, Yesu anaimirira nafuula, ndi kunena, Ngati pali munthu akumva ludzu, adze kwa Ine, namwe.