Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 143:11 - Buku Lopatulika

Mundipatse moyo, Yehova, chifukwa cha dzina lanu; mwa chilungamo chanu mutulutse moyo wanga m'sautso.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Mundipatse moyo, Yehova, chifukwa cha dzina lanu; mwa chilungamo chanu mutulutse moyo wanga m'sautso.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Sungani moyo wanga, Inu Chauta, kuti dzina lanu lilemekezeke. Munditulutse pa mavuto chifukwa cha kulungama kwanu.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Sungani moyo wanga Inu Yehova chifukwa cha dzina lanu; mwa chilungamo chanu tulutseni mʼmasautso anga.

Onani mutuwo



Masalimo 143:11
19 Mawu Ofanana  

Ndazunzika kwambiri: Ndipatseni moyo, Yehova, monga mwa mau anu.


Moyo wanga umamatika ndi fumbi; mundipatse moyo monga mwa mau anu.


Muchititse mlubza maso anga ndisapenye zachabe, mundipatse moyo mu njira yanu.


Taonani, ndinalira malangizo anu; mundipatse moyo mwa chilungamo chanu.


Mundipatse moyo monga mwa chifundo chanu; ndipo ndidzasamalira mboni ya pakamwa panu.


Ndingakhale ndiyenda pakati pa nsautso, mudzandipatsa moyo; mudzatambasula dzanja lanu pa mkwiyo wa adani anu, ndipo dzanja lanu lamanja lidzandipulumutsa.


Imvani pemphero langa, Yehova; nditcherere khutu kupemba kwanga; ndiyankheni mwa chikhulupiriko chanu, mwa chilungamo chanu.


Chifukwa cha dzina lanu, Yehova, ndikhululukireni kusakaza kwanga, pakuti ndiko kwakukulu.


Masautso a mtima wanga akula, munditulutse m'zondipsinja.


Ndakhulupirira Inu, Yehova, ndikhale wopanda manyazi nthawi zonse, mwa chilungamo chanu ndipulumutseni ine.


Masautso a wolungama mtima achuluka, koma Yehova amlanditsa mwa onsewa.


Ndikwatuleni m'chilungamo chanu, ndi kundilanditsa, nditcherereni khutu lanu ndi kundipulumutsa.


Kodi simudzatipatsanso moyo, kuti anthu anu akondwerere ndi Inu?


Yehova, ndinamva mbiri yanu ndi mantha; Yehova, tsitsimutsani ntchito yanu pakati pa zaka, pakati pa zaka mudziwitse; pa mkwiyo mukumbukire chifundo.