Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 139:13 - Buku Lopatulika

Pakuti Inu munalenga impso zanga; munandiumba ndisanabadwe ine.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Pakuti Inu munalenga impso zanga; munandiumba ndisanabadwe ine.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Paja ndinu mudapanga za m'kati mwanga, mudandiwumba m'mimba mwa amai anga.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Pakuti Inu munalenga za mʼkati mwanga; munandiwumba pamodzi mʼmimba mwa amayi anga.

Onani mutuwo



Masalimo 139:13
10 Mawu Ofanana  

Kodi Iye amene anandilenga ine m'mimba sanamlenge iyenso? Sindiye mmodzi anatiumba m'mimba?


Manja anu anandilenga nandiumba; mundizindikiritse, kuti ndiphunzire malemba anu.


Inu munandigwiriziza kuyambira ndisanabadwe, kuyambira pa thupi la mai wanga wondichitira zokoma ndinu; ndidzakulemekezani kosalekeza.


Tiyeni, tipembedze tiwerame; tigwade pamaso pa Yehova, amene anatilenga.


atero Yehova, amene anakutenga iwe, nakuumba kuchokera m'mimba, amene adzathangata iwe. Usaope Yakobo, mtumiki wanga ndi iwe, Yesuruni, amene ndakusankha iwe.


Mverani Ine, banja la Yakobo, ndi otsala onse a banja la Israele, amene ndakunyamulani kuyambira m'mimba, ndi kukusenzani chibadwire;


Ndisanakulenge iwe m'mimba ndinakudziwa, ndipo usanabadwe ndinakupatula iwe; ndinakuika kuti ukhale mneneri wa mitundu ya anthu.


Ngati thupi lonse likadakhala diso, kukadakhala kuti kununkhiza?