Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 137:9 - Buku Lopatulika

Wodala iye amene adzagwira makanda ako, ndi kuwaphwanya pathanthwe.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Wodala iye amene adzagwira makanda ako, ndi kuwaphwanya pathanthwe.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Adzakhala wodala munthu amene adzatenga makanda ako ndi kuŵakankhanthitsa ku thanthwe.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Amene adzagwira makanda ako ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.

Onani mutuwo



Masalimo 137:9
5 Mawu Ofanana  

Nati Hazaele, Muliriranji, mbuye wanga? Nayankha iye, Popeza ndidziwa choipa udzachitira ana a Israele; udzatentha malinga ao ndi moto, nudzapha anyamata ao ndi lupanga, nudzaphwanya makanda ao, nudzang'amba akazi ao okhala ndi pakati.


Makanda ao adzatswanyidwe pamaso pao; m'nyumba mwao mudzafunkhidwa, ndi akazi ao adzakakamizidwa.


Momwemo phokoso lidzaukira anthu ako, ndi malinga ako onse adzapasuka, monga Salimani anapasula Betaribele; tsiku la nkhondo amai anaphwanyika pamodzi ndi ana ake.


Samariya adzasanduka wabwinja, pakuti anapandukana ndi Mulungu wake; iwo adzagwa ndi lupanga, ana ao amakanda adzaphwanyika, ndi akazi ao okhala ndi pakati adzatumbulidwa.


Koma iye anatengedwa, analowa ndende; ana ake a makanda anaphwanyika polekeza pake pa miseu yake yonse; ndi pa omveka ake anachita maere, ndi akulu ake onse anamangidwa maunyolo.