Masalimo 137:2 - Buku Lopatulika Pa msondodzi uli m'mwemo tinapachika mazeze athu. Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 Pa msondodzi uli m'mwemo tinapachika mazeze athu. Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa Kumeneko tidapachika apangwe athu pa mitengo ya misondodzi. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Kumeneko, pa mitengo ya misondozi tinapachika apangwe athu, |
Kusangalala kwa mangaka kwalekeka, phokoso la iwo amene asekera litha, kukondwa kwa mngoli kwalekeka.
Ndipo ndidzasanduliza zikondwerero zanu zikhale maliro, ndi nyimbo zanu zikhale za maliro, ndi kufikitsa ziguduli m'chuuno monse, ndi mpala pamutu uliwonse; nadzakhala ngati maliro a mwana mmodzi yekha, ndi chitsiriziro chake ngati tsiku lowawa.
Ndipo mau a anthu oimba zeze, ndi a oimba, ndi a oliza zitoliro, ndi a oomba malipenga sadzamvekanso konse mwa iwe; ndipo mmisiri aliyense wa machitidwe ali onse sadzapezedwanso konse mwa iwe; ndi mau a mphero sadzamvekanso konse mwa iwe;