Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 136:6 - Buku Lopatulika

Amene anayala dziko lapansi pamwamba pamadzi; pakuti chifundo chake nchosatha.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Amene anayala dziko lapansi pamwamba pa madzi; pakuti chifundo chake nchosatha.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Adayala dziko lapansi pa madzi, pakuti chikondi chake nchamuyaya.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Amene anayala dziko lapansi pamwamba pa madzi, pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

Onani mutuwo



Masalimo 136:6
11 Mawu Ofanana  

Ndipo anati Mulungu, Madzi a pansi pakumwamba asonkhane pamodzi pamalo amodzi, uoneke mtunda: ndipo kunatero.


Ayala kumpoto popanda kanthu, nalenjeka dziko pachabe.


Kodi muyala thambo pamodzi ndi Iye, ndilo lolimba ngati kalirole woyengeka?


Pakuti Iye analimanga pazinyanja, nalikhazika pamadzi.


Ndi Iye amene akhala pamwamba pa malekezero a dziko lapansi, ndipo okhalamo akunga ziwala; amene afutukula thambo ngati chinsalu, naliyala monga hema wakukhalamo;


Atero Mulungu Yehova, Iye amene analenga thambo, nalifutukula, nayala ponse dziko lapansi, ndi chimene chituluka m'menemo, Iye amene amapatsa anthu a m'menemo mpweya, ndi mzimu kwa iwo amene ayenda m'menemo;


Atero Yehova, Mombolo wako, ndi Iye amene anakuumba iwe m'mimba, Ine ndine Yehova, amene ndipanga zinthu zonse, ndi kufunyulula ndekha zakumwamba, ndi kuyala dziko lapansi; ndani ali ndi Ine?


Iye analenga dziko lapansi ndi mphamvu yake, nakhazikitsa dziko lapansi ndi nzeru yake, nayala thambo ndi kuzindikira kwake;


Katundu wa mau a Yehova wakunena Israele. Atero Yehova, wakuyala miyamba, ndi kuika maziko a dziko lapansi, ndi kulenga mzimu wa munthu m'kati mwake;