Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 136:5 - Buku Lopatulika

Amene analenga zakumwamba mwanzeru; pakuti chifundo chake nchosatha.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Amene analenga zakumwamba mwanzeru; pakuti chifundo chake nchosatha.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Adalenga zakumwamba ndi nzeru zake, pakuti chikondi chake nchamuyaya.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Amene mwachidziwitso chake anapanga mayiko akumwamba, pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

Onani mutuwo



Masalimo 136:5
11 Mawu Ofanana  

Pachiyambi Mulungu adalenga kumwamba ndi dziko lapansi.


Ndipo Mulungu anapanga thambo, nalekanitsa madzi anali pansi pathambolo ndi madzi anali pamwamba pathambolo; ndipo kunatero.


Ndipo Mulungu analitcha thambolo Kumwamba. Ndipo panali madzulo ndipo panali m'mawa, tsiku lachiwiri.


Ntchito zanu zichulukadi, Yehova! Munazichita zonse mwanzeru; dziko lapansi lidzala nacho chuma chanu.


Yehova, ali mu Ziyoni, akudalitseni; ndiye amene analenga kumwamba ndi dziko lapansi.


Zakumwamba zinalengedwa ndi mau a Yehova; ndipo ndi mpweya wa m'kamwa mwake khamu lao lonse.


munthu ndani kuti mumkumbukira? Ndi mwana wa munthu kuti mucheza naye?


Iye analenga dziko lapansi ndi mphamvu yake, nakhazikitsa dziko lapansi ndi nzeru yake, nayala thambo ndi kuzindikira kwake;


Iye analenga dziko lapansi ndi mphamvu yake, wakhazika dziko lapansi ndi nzeru yake, ndi luso anayala thambo;