Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 136:10 - Buku Lopatulika

Iye amene anapandira Aejipito ana ao oyamba; pakuti chifundo chake nchosatha.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Iye amene anapandira Aejipito ana ao oyamba; pakuti chifundo chake nchosatha.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Adapha ana achisamba a ku Ejipito, pakuti chikondi chake nchamuyaya.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Amene anakantha ana woyamba kubadwa a Igupto, pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

Onani mutuwo



Masalimo 136:10
8 Mawu Ofanana  

Ndipo Iye anapha achisamba onse m'dziko mwao, choyambira cha mphamvu yao yonse.


Anapanda oyamba a Ejipito, kuyambira munthu kufikira zoweta.


Ndipo anapha ana oyamba onse a mu Ejipito, ndiwo oyamba a mphamvu yao m'mahema a Hamu.


Pakuti ndidzapita pakati padziko la Ejipito usiku womwewo, ndi kukantha ana oyamba onse m'dziko la Ejipito, anthu ndi zoweta; ndipo ndidzachita maweruzo pa milungu yonse ya Aejipito; Ine ndine Yehova.


Ndipo panakhala pakati pa usiku, Yehova anakantha ana oyamba onse a m'dziko la Ejipito, kuyambira mwana woyamba wa Farao wakukhala pa mpando wachifumu wake kufikira mwana woyamba wa wam'nsinga ali m'kaidi; ndi ana oyamba onse a zoweta.


Ndipo mtundu umene udzawayesa akapolo, ndidzauweruza Ine, anatero Mulungu; ndipo zitapita izi adzatuluka, nadzanditumikira Ine m'malo muno.


Ndi chikhulupiriro anachita Paska, ndi kuwaza kwa mwazi, kuti wakuononga ana oyamba angawakhudze iwo.